Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Tiwapatsa mwayi wa ngongole kuti apeze mpamba — TEVETA

Pofuna kuwonetsetsa kuti achinyamata amene amaliza maphunziro a ulimi wa zipatso, masamba, maluwa ndi mbewu zina pa sukulu ya Corporate Institute of Horticulture (CIH) ali ndi mpamba oyambira malonda, bungwe la Technical Entrepreneurial and Vocational Education and Training Authority (TEVETA) lagwirizana ndi banki ya FDH kudzanso bungwe la National Economic Empowerment Fund (NEEF) kuti lithandize anyamata omwe amaliza maphunziro ndi ngongole.

Mkulu wa bungwe la TEVETA m’chigawo cha pakati, a Joseph Sambaya, anena izi m’boma la Salima pomwe amapereka ma satifiketi kwa achinyamata omwe amaliza maphunziro a ulimi wa zipatso pa sukuluyo.

Peter Mlangali, mmodzi mwa ophunzira omwe amaliza maphunziro, wati ngongoleyi ithandiza achinyamatawa kupeza nawo mwayi wochita malonda pa misika ya m’dziko muno ndi misika yakunja kamba koti akhala ndi mpamba okwanira.

 

Wolemba Aisha Amidu

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Zomba farmers on a learning visit in Nkhotakota

MBC Online

EAM WANTS LEGISLATORS TO GET SERIOUS

Kumbukani Phiri

Bullets look to seal the deal against Arrows

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.