Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Tikupha makwacha – TAMA

Bungwe la alimi a fodya la Tobacco Association of Malawi (TAMA) Trust lati alimi a fodya ndiwokondwa chaka chino kamba koti akupha makwacha ndi mitengo yabwino yafodya yomwe ogula akupereka.

Mtsogoleri wa TAMA, a Abel Kalima Banda, awuza MBC Digital kuti chiyambireni msikawu chaka chino, mitengo yakhala ikukwera.

Iwo alonjeza kuti alimi apitiriza kupititsa fodya wabwino ku msikawu.

Pakutha sabata zisanu ndi ziwiri, alimi mdziko muno apeza ndalama zokwana K327 billion kuchokera ku fodya.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Namondwe sakhalapo koma mvula yamphamvu m’madera ena — MET

MBC Online

Chitukuko chifalikira m’boma lonse la Nsanje — Zikhale

Arthur Chokhotho

Tisafalitse zopanda umboni

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.