Malawi Broadcasting Corporation
Entertainment Local News Nkhani

“Tidzikondana tili moyo”

“Ndikofunika kuti a Malawi adzikondana komanso kuthandizana pa mavuto ndi mtendere,” awa ndi mawu amene anena ndi eni ake a kampani ya Sosten Motors, a Sosten Kapeni.

Iwo amayankhula izi pamene amachingamira katswiri ojambula zithunzi m’dziko muno, Ras Peter Kansengwa, pa bwalo la ndege la Kamuzu mu mzinda wa Lilongwe.

Kansengwa adali m’dziko la India kumene amalandira thandizo pa chipatala cha Artemis.

A Kapeni apereka ndalama yokwana K500,000 kwa a Kansegwa kuti adzigwiritsa ntchito pa moyo wawo.

“Zimakhala zokhudza kuona anthu akuthandiza kwambiri pamwambo wa maliro, chonsecho munthu wakhala akuvutika ali moyo,” iwo anatero.

Ras Kansengwa anayamikira boma komanso aMalawi amene akhala akuwathandiza pamene adali m’chipatala kulandira thandizo kwa mwezi ndi theka.

M’mbuyomu, iwo adalinso m’dziko la India kumene adakalandira opaleshoni ya diso.

 

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

Nyambose quits as Bangwe Coach!

MBC Online

Chakwera to visit flood victims, inspect irrigation schemes in KA

Romeo Umali

Tremour’s family to release posthumous song on Made on Monday

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.