Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

President Chakwera awonekera m’nyumba ya malamulo

Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, lero akawonekera ku nyumba ya malamulo ndikukayankha mafunso kuchokera kwa aphungu anyumbayi.

Potsimikiza izi, mneneri wa Boma, a Moses Kunkuyu, wati President Chakwera akawonekera ku nyumbayi pokwaniritsa malonjezo ake woti adzakhala wotumikira anthu a m’dziko muno poyankha mafunso kudzera kwa aphungu awo.

Mtsogoleri wadziko linoyu akakhala ali ku nyumba ya malamulo masana ano kuyambira nthawi ya 2 koloko.

Wolemba: Timothy Kateta

#MBCOnlineServices

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

South West Region sees surge in homicide, theft cases

Romeo Umali

MALAWI SECURES $100 MN FOR STUDENTS’ LOANS

Blessings Kanache

MALAWI TO LEAD AMCOW ACTIVITIES

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.