Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

President Chakwera awonekera m’nyumba ya malamulo

Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, lero akawonekera ku nyumba ya malamulo ndikukayankha mafunso kuchokera kwa aphungu anyumbayi.

Potsimikiza izi, mneneri wa Boma, a Moses Kunkuyu, wati President Chakwera akawonekera ku nyumbayi pokwaniritsa malonjezo ake woti adzakhala wotumikira anthu a m’dziko muno poyankha mafunso kudzera kwa aphungu awo.

Mtsogoleri wadziko linoyu akakhala ali ku nyumba ya malamulo masana ano kuyambira nthawi ya 2 koloko.

Wolemba: Timothy Kateta

#MBCOnlineServices

Related posts

Malawi narrows trade deficit – RBM

Rabson Kondowe

Ministry of Trade lauds cooperatives for boosting economy

Rabson Kondowe

Ministry of Local Govt urges councils to accelerate project implementation

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.