Malawi Broadcasting Corporation
Education Nkhani

Palibe mtsikana abwezedwe ku MUST chifukwa cha fizi — Prof. Malata

Wachiwiri kwa Chancellor wa sukulu ya ukachenjede ya Malawi University of Science and Technology (MUST), Professor Address Malata, wati atsikana onse omwe anawasankhira ku sukuluyi ndipo analephera kuyamba maphunziro chifukwa cha kusowa kwa ndalama zolipilira sukulu apite akayambe chifukwa ndalama zapezeka.

Professor Malata auza MBC kuti zoti atsikana adzisiya sukulu chifukwa chosowa malipiro MUST siikupanga nawo.

Iwo anena izi pamene kampani ya Illovo Sugar Malawi imaperaka ndalama zokwana K250 million ku thumba lothandizira ophunzira osowa, makamaka atsikana.

Iwo ati padakali pano, kuthumbali kuli ndalama zokwana K400 million.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Mabanker ndi Manoma : Wamkulu ndani?

Emmanuel Chikonso

MUBAS holds Research, Innovation Week

Chisomo Break

Nyimboyi ithandize onse osweka mitima – Sife Mw

Emmanuel Chikonso
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.