Malawi Broadcasting Corporation
Local

Okuba chimanga cha ADMARC awamanga

A polisi amanga munthu mmodzi ogwira ntchito ku bungwe la ADMARC ndi ena awiri powaganizila kuti anazembetsa matumba a chimanga okwana 300 m’boma la Machinga.

Ofalitsa nkhani za apolisi mchigawo chakumvuma,  a Patrick Mussa,  ati amanga a Malani Kaira a zaka 35 a ku bungweli, komanso a  Isaac Bisayi a zaka 39 komanso a Imran Mtambo a zaka 30.

A Mussa ati a Bisayi omwe ndi dalaivala wa galimoto yaikulu, anapachila matumba achimanga okwana 600 kuchokera pa ADMARC ya Dowa, omwe amayenela kukawatsitsa ku Nkwepele m’bomali, koma mmalo mwake anakatsitsa matumba 300 pakhomo pa Imran Ntonda ku Ntaja.

Iwo ati atatuwa, awatsegulira mulandu ogwirizana pofuna kuba komanso wina okuba.

#mbconlineservices

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Death-toll rises to three in Dedza road accident

Sothini Ndazi

Man sentenced to 21 years in jail for murder, robbery

Romeo Umali

CHAKWERA INSPIRES HOPE AGAINST  HUNGER

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.