Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Technology

Ntchito za ICT ndi zandalama — Kunkuyu

Nduna ya Zofalitsa nkhani, a Moses Kunkuyu, yayamika m’modzi mwa anthu ochita malonda pa luso la makono (ICT), a Wisely Phiri, amene ndi mwini wake wa Sparc Systems, kaamba komanga nyumba ya makono kwambiri munzinda wa Lilongwe.

A Kunkuyu ati zimene achita a Phiri ndi umboni okuti mu ntchito za ICT muli ndalama zimene zingathandize pa chitukuko cha dziko lino.

Iwo anati nthawi zambiri a Malawi amaziyang’anira pansi m’malo mochita zinthu zothandiza kutchukitsa dziko lino.

A Phiri anati alinso ndi mapulani omanga sukulu yophunzitsa ICT ku Blantyre komanso mayiko a Zambia ndi Mozambique.

Iwo apempha boma kuti lidzipereka ma contract ambiri kwa a business achi Malawi pofuna kulimbikitsa aMalawiwo pa ntchito zokweza dziko lino.

Sparc Systems Limited adayikhazikitsa 2013 ndipo ili ndi ofesi kuno ku Malawi, Zambia ndi Rwanda.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Kunkuyu represents Chakwera at Kapoloma’s funeral

MBC Online

OVER 2,000 YOUTHS EMPOWERED WITH DIGITAL AND ENTREPRENEURIAL SKILLS

Lonjezo Msodoka

MABEDI SPEAKS ON PERMANENT COACHING ROLE

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.