Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Technology

Ntchito za ICT ndi zandalama — Kunkuyu

Nduna ya Zofalitsa nkhani, a Moses Kunkuyu, yayamika m’modzi mwa anthu ochita malonda pa luso la makono (ICT), a Wisely Phiri, amene ndi mwini wake wa Sparc Systems, kaamba komanga nyumba ya makono kwambiri munzinda wa Lilongwe.

A Kunkuyu ati zimene achita a Phiri ndi umboni okuti mu ntchito za ICT muli ndalama zimene zingathandize pa chitukuko cha dziko lino.

Iwo anati nthawi zambiri a Malawi amaziyang’anira pansi m’malo mochita zinthu zothandiza kutchukitsa dziko lino.

A Phiri anati alinso ndi mapulani omanga sukulu yophunzitsa ICT ku Blantyre komanso mayiko a Zambia ndi Mozambique.

Iwo apempha boma kuti lidzipereka ma contract ambiri kwa a business achi Malawi pofuna kulimbikitsa aMalawiwo pa ntchito zokweza dziko lino.

Sparc Systems Limited adayikhazikitsa 2013 ndipo ili ndi ofesi kuno ku Malawi, Zambia ndi Rwanda.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

ESCOM, MEAP project to connect over 90,000 customers by June

Arthur Chokhotho

Phase three to cover eight councils- MEC

MBC Online

MNCS suspends sporting activities to mourn Chilima

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.