Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani Sports

Nkhani sindalama koma zomwe Bullets yachita – Silver Strikers

Mkulu wa timu ya Silver Strikers Patrick Chimimba wati chidwi chikhale pa zomwe Bullets yachita povomereza ndikupepesa ku timu ya Silver osati ndalama zomwe apereka.

A Chimimba auza MBC kuti makoteshoni omwe Bullets inapempha itavomera zokonzetsa bus anadutsa K10 million ndipo pakadali pano alandira K6 million.

“Mmene ndanenera nkhani ikhale zomwe Bullets yachita chifukwa ndimatimu ochepa omwe angapange izi kubwera kudzapepesa timu yomwe ayilakwira,” atero a Chimimba, poonjezera kuthokoza kwawo ku timu ya Bullets chifukwa cha kudzichepetsa.

Malinga ndi a Chimimba Bullets yawonetsa ukulu, ponena kuti ndi ochepa amabwera poyera ndikuvomera kulakwitsa kwawo.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Gulu la alimi lapeza K620 million kudzera mu ulimi wa nzimbe

Doreen Sonani

Bullets finish 4th in Super League First Round

Romeo Umali

‘Andale ena akumatenga anthu ammadera akutali kudzawalembetsa mkaundula wa voti’

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.