Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Sports Sports

Ndimugwetsa ndime yoyamba, Visser achenjeza

 

Katswiri wa nkhonya ochokera m’dziko la South Africa, Ruann Visser, wati iye akong’ontha ndi kugwetsa Mussa Ajibu, amene ndi katswiri wa zigogodo wa m’dziko muno, mu ndime yoyamba mwa zisanu ndi zitatu zimene akuyenera kumenyana.

Visser, yemwe ndi wamtali mododometsa, anayankhula izi atangofika m’dziko muno pa bwalo la ndege la Kamuzu mumzinda wa Lilongwe pamodzi ndi katswiri wina Francy Ntetu wa m’dziko la Democratic Republic of Congo (DRC).

Ntetu, amene amayimilira dziko la Canada, awonetsana chamuna ndi namandwa pa nkhonya m’dziko muno, Alick Mwenda.

“Ndine ochezeka ndi kakhala kunja kwa ring koma ndi kalowa mu ring ndimasintha mawanga,” anachenjeza Ntetu.

Youth Boxing Promotion ndi imene yakonza masewerowa amene achitike Lamulungu ku Lilongwe ku Area 36.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Apolisi agwira mayi atamenya ogwira ntchito mu ndege

Mayeso Chikhadzula

Chakwera hails USAID for supporting Malawi’s SDGs

Mayeso Chikhadzula

Gonapamuhanya Cultural Festival to advance women, youth interest

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.