Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Ndife okondwa kuti boma limatiika mmapulani ake – Ras Mwanamanga

Wachiwiri kwa nduna yaza ulimi Benedicto Chambo anacheza ndi akuluakulu achipembezo chachi Rasta munzinda wa Lilongwe.

A Chambo, omwenso ndi phungu wadera la Mangochi – Makanjira, ati ma rasta ndi anthu ofunikira kwambiri pa chitukuko cha dziko lino choncho akufunika osamawssiya mmbuyo pokwaniritsa masomphenya a Malawi 2063.

Iwo ati ichi ndichifukwa chake mtsogoleri wa dziko lino amaonetsetsa kuti aliyense adzitha kukhala ndi mwayi okhala m’maudindo osiyanasiyana ofunikira.

Ras elder Mwanamanga, yemwenso ndi mmodzi mwa atsogoleri ku mpingo wachi Rasta Ku Nyabingi House ku Area 17 munzinda wa Lilongwe, wati ndi okondwa kuti boma layika padera mapologalamu osiyanasiyana omwe cholinga chake nkusintha miyoyo ya anthu m’dziko muno.

Lachisanu pomwe aphungu amamaliza msonkhano wawo, ma rasta anali nawo kunyumbayi kutsatira zokammbiranazi.

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

Brands Africa gives back to customers

Kumbukani Phiri

‘Tisalore katangale pa ntchito zaumoyo’

MBC Online

PRISAM lauds Chakwera’s move to increase student allowances

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.