Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Mwala otayidwa unasanduka mwala wapangodya, watero Msonda

A Ken Msonda, omwe alandiridwa ku chipani cha Malawi Congress MCP dzulo, ati ndi odabwitsidwa ndi chilimbikitso chimene apatsidwa ndi mafumu akuluakulu a m’boma la Rumphi pamene alowa m’chipanichi.

Iwo ati sizinachitikepo mu mbiri ya ndale m’dziko muno mafumu kuperekeza munthu kukalowa chipani.

Polowa m’chipani cha MCP, a Ken Msonda anaperekezedwa ndi mafumu motsogozedwa ndi Paramount Chief Chikulamayembe komanso m’busa Victor Chikhosa wa mpingo wa Chiweta CCAP, mwa ena.

“Ambuye watseka pakamwa onse wotukwana, wolalata, wonyoza,” atero a Msonda.

By Blessings Cheleuka

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Mwambo wa Sand Music siukhalapo chaka chino

Simeon Boyce

A Chakwera acheza ndi ochita malonda kunyumba ya boma

MBC Online

Ntchito yogula magetsi ku Mozambique yatsala pang’ono kuyamba

Justin Mkweu
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.