Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MRA ibwezera alimi afodya K9.4 billion

Alimi a fodya ayamikira boma komanso bungwe lotolera misonkho la Malawi Revenue Authority (MRA) powabwezera ndalama zokwana K9. 4 billion zamsonkho omwe akhala akudulidwa  akagulitsa fodya ku msika wovomerezeka wa fodya.

Izi zadziwika  pamsonkhano wa alimiwa mumzinda wa Lilongwe.

Oimira alimiwa, GVH Kasangazi ati zomwe lachita bungwe la MRA zawonetsera poyera kuti boma likufuna kuti alimi adzipindula pantchito yawo, ponena kuti alimiwa samadziwa msonkho woyenera kuti adulidwe.

Wachiwiri kwa komishonala wa bungwe la MRA, a Janet Kholowa, ati boma laika ndondomeko yatsopano yoti alimiwa asamavutike ndikubwera kumaofesi a bungweli kuti abwezeredwe ndalama.

“Mukhoza kuona kuti pa makalabu 14,800 ndiye kuti ndi alimi osachepera 148,000 omwe timayenera tiunike ngati anapeza phindu kapena ayi tisanawabwezere ndalama. Koma tsopano kuyambira mchaka cha 2021 tikungodula 1 percent ndipo tikatero tathana,” anatero a Kholowa.

Ndalama yokwana K14.9 billion ikubwezeredwa kwa alimi ochokera m’makalabu 14800 m’dziko muno, omwe akhala akudulidwa msonkho kuyambira m’chaka cha 2014 mpaka 2020.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Chimwendo drums up support for MCP candidate in Chilanga Ward

Mayeso Chikhadzula

Mabedi confident of his charges

MBC Online

MAGLA to build a sports arena at Likhubula

Jeffrey Chinawa
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.