Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Religion

M’busa apempha anthu kuti athandize osowa

Atsogoleri amipingo ati nkofunika kuti anthu adzipereka thandizo kwa iwo ovutika potsatira mavuto omwe ambiri m’dziko muno akukumana nawo.

M’busa Bishop William Mandhlopa a mpingo wa Family of God International anayankhula izi ku Area 44 mumzinda wa Lilongwe pamwambo opereka nyumba kwa bambo ndi mai George Phiri, amene ndi abusa opuma a mpingo wa Holy Ghost ndipo ndi okalamba.

Iwo anati chimene achitachi chikhale chilimbikitso kwa anthu kuti adzipereka thandizo kwa iwo ovutika.

M’mau awo, bambo ndi mai Phiri anayamika kwambiri m’busayo kaamba ka nyumbayi, ponena kuti moyo okhala pa rent unali ovuta.

Nyumbayo yamangidwa ndi ndalama zokwana K8 million.

#MBCOnlineServices

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

First Lady’s Shaping the Future Foundation Hosts Fundraising Dinner at Kamuzu Palace

MBC Online

President Chakwera hints at new international support for Social Cash Transfer Programme

Earlene Chimoyo

Mabungwe ayamika boma poyendetsa bwino chuma

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.