Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MBC ikuchita bwino — Chiyamwaka

Unduna wazofalitsa nkhani wati ndiokhutira ndi m’mene MB ikugwirira ntchito zake  pokwaniritsa zokhumba za aMalawi onse m’dziko muno.

Mlembi wamkulu mu undunawu, a Baldwin Chiyamwaka, ati ndizosangalatsa kuti madandaulo amene anthu mmbuyomu anali nawo pa mapologalamu a MBC tsopano anachepa kwambiri, kutanthauza kuti bungweli likuyesetsa.

A Chiyamwaka anena izi atayendera maofesi a MBC ku Blantyre ndikuona zipangizo zomwe MBC ikugwiritsa ntchito powulutsa mawu.

Iwo ati undunawu upitiriza kuthandiza MBC munjira zosiyanasiyana kuti ikwaniritse zolinga zake zofikira aMalawi onse.

 

Related posts

FOMO stuns KB, Bullets move 5th

Romeo Umali

Kusankhidwa kwa Justice Mtalimanja kulimbikitsa atsikana, amayi — Undule

Romeo Umali

OXFAM yaika padera K650m yothandizira amayi pandale

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.