Phungu wa dera la Lilongwe Msinja South, Francis Belekanyama, watsindika zakufunika kokhazikitsa ntchito zomwe zimathandiza achinyamata kupeza zochita.
Belekanyama walankhula izi pasukulu ya pulaimale ya Matsimbe mdera lamfumu yayikulu Masula Ku Lilongwe pamwambo opereka mphoto kwa omwe apambana pamapeto pa masewero amu Belekanyama Bonanza.
Iwo anati kukhazikitsa ntchito ngati mpikisano wa mpira wamiyendo komanso wamanja zimathandiza achinyamata kupeza zochita ndikulewa makhalidwe oipa.
M’mawu ake, wapampando wachipani cha Malawi Congress (MCP) mchigawo chapakati, a Patrick Zebron Chilondola, anayamikira phunguyu pokhazikitsa zikho kudera lake.
Iwo anati phungu akakhala pampando amayenera adzigwira ntchito zotukula miyoyo ya anthu omwe anamuika pampando wake.
Pakali pano, a Belekanyama akhazikitsanso mpikisano wina wachikho cha mpira wa manja ndi miyendo cha K6 million.
#MBCDigital
#Manthu