Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Business Development Local News Nkhani

Malawi yapeza $2 million kuchokera ku Israel

Photo Credit : Gianluigi Guercia

Pofika mwezi uno, dziko la Malawi lapeza ndalama zokwana $2 million (pafupifupi K3.4 billion) kuchoka ku ndondomeko yotumiza achinyamata kukagwira ntchito mu dziko la Israel.

Izi ndi malingana ndi nduna yowona zachuma, a Simplex Chithyola Banda.

A Chithyola Banda ati pakutha pa mwezi uno, akuyembekezera kuti dziko lino likhala litapeza $1 million (pafupifupi K1.7 billion) yowonjezera.

Iwo ati izi zikuthandiza dziko lino kumbali yopeza ndalama zakunja mosavuta.

Related posts

Tigers claim bitter-sweet 3 points

Romeo Umali

MHRC hails MEC for orderly 16 September polls

Romeo Umali

Elderly man drowns in well

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.