Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

MAKHANSALA AWIRI A DPP ALOWA MCP KU PHALOMBE

Makhansala awiri a chipani cha Democratic Progressive (DPP) atuluka mchipanichi  ndipo alowa cha Malawi Congress (MCP).

Mkulu okopa anthu mu MCP a Moses Kunkuyu  alandila makhansala awiriwa pa msonkhano omwe anachititsa pa sukulu ya Chilayeni m’dera la Sub TA Nyambalo ku Phalombe.

Makhansalawa ndi a Felix Blair Jumbe a Mauzi ward mdera la Phalombe North East, komanso a Fedison Thomas a dera la Likulezi Ward kum’mwera kwa Phalombe.

Makhansalawa omwe anabwela ndi mafumu a m’maderawa ati achita izi kaamba Prezidenti Dr Lazarus Chakwera ndi okhululuka komanso chipani chawo ndi cha mtendere ndipo akufuna chitukuko.

 

Related posts

‘Boma lithandiza onse’

Romeo Umali

Kusankhidwa kwa Justice Mtalimanja kulimbikitsa atsikana, amayi — Undule

Romeo Umali

‘Boma liteteze atsikana nthawi ya ngozi zadzidzidzi’

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.