Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

MAKHANSALA AWIRI A DPP ALOWA MCP KU PHALOMBE

Makhansala awiri a chipani cha Democratic Progressive (DPP) atuluka mchipanichi  ndipo alowa cha Malawi Congress (MCP).

Mkulu okopa anthu mu MCP a Moses Kunkuyu  alandila makhansala awiriwa pa msonkhano omwe anachititsa pa sukulu ya Chilayeni m’dera la Sub TA Nyambalo ku Phalombe.

Makhansalawa ndi a Felix Blair Jumbe a Mauzi ward mdera la Phalombe North East, komanso a Fedison Thomas a dera la Likulezi Ward kum’mwera kwa Phalombe.

Makhansalawa omwe anabwela ndi mafumu a m’maderawa ati achita izi kaamba Prezidenti Dr Lazarus Chakwera ndi okhululuka komanso chipani chawo ndi cha mtendere ndipo akufuna chitukuko.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Tilimbikitse ulimi wa mthilira – Kawinga

MBC Online

‘Osakakamira wachikondi wankhanza’

Paul Mlowoka

Okhupha mnzake amugwira

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.