Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Lolemba ndi tchuthi’

Nduna yazofalitsa nkhani , a Moses Kunkuyu, ati  mtsogoleri wa dziko lino, Dr. Lazarus Chakwera, alamula kuti lolemba likudzali, limene lili tsiku loyika mmanda ku Ntcheu yemwe anali wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko, malemu Dr Saulos Chilima, likhale tsiku la tchuthi.

Iwo ati cholinga chake ndikufuna kuti aMalawi athe kulira maliro a Dr. Chilima.

A Kunkuyu alongosola izi kumsonkhano wa olembankhani kunyumba yamalamulo.

Mmau awo, iwo ati ku mwambowu kukapezekanso akuluakulu osiyanasiyana ochokera kunja kwa dziko lino monga ku Tanzania, Botswana ndi Mozambique.

 

Olemba Mirriam Kaliza

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Mkandawire calls for more support towards war veterans

Nobert Jameson

Cha Cha funds waiting shelter at Lingadzi Police Station

McDonald Chiwayula

Apalasa kuchoka Lilongwe mpaka Blantyre pofuna kutolera K100 million

Emmanuel Chikonso
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.