Malawi Broadcasting Corporation
Local News

Kuli ufulu wa demokalase ku MCP— Chilondola

Wapampando wa chipani cha Malawi Congress Party (MCP) m’chigawo chapakati, a Patrick Zebron Chilondola, wati ufulu wopikisana pa maudindo wosiyanasiyana kumene kulipo ndi chitsimikizo kuti chipanichi chimalemekeza ufulu wa demokalase.

Poyankhula ndi MBC pa Madisi Trading Centre pomwe mtsogoleli wadziko lino Dr Lazarus Chakwera anaima kupeleka moni kwa khwimbi lomwe linasonkhana pa malowa lolemba, a Chilondola anati MCP ndi chipani cha dziko lonse.

Pamasamba a mchezo pakhala pakuyenda zithunzi za anthu osiyanasiyana amene anthu akuwaikapo ngati oyenelera  kudzatsogolela pa maudindo osiyanasiyana ku chipani cha MCP.

Mlembi wamkulu wa chipani cha MCP, a Eisenhower Mkaka, anati zikusonyezeratu kuti akuluakulu achipanichi ndi mamembala onse akugwirizana kwathunthu kuti Dr Chakwera, yemwenso ndi Prezidenti wa chipani cha MCP, ndiye adzaimire chipanichi pa chisankho cha 2025.

Chipani cha MCP chikuyembekeza kuchititsa msonkhano wake waukulu (convention) m’mwezi wa August chaka chino.

Anthu amene adzasankhidwe akuyembekezeka kudzatsogolera chipanichi kwa zaka zisanu.

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

MAGU launches pre-schoolers’ book

MBC Online

MANEPO hails passing of Older Persons’ Bill

MBC Online

Maize restocking exercise on track – ADMARC

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.