Khonsolo ya mnzinda wa Lilongwe yati ndi yodzipereka pa ntchito yolimbikitsa bata ndi mtendere m’dziko muno.
Wachiwiri kwa mfumu ya mnzinda wa Lilongwe, a Ruth Njirayafa, ayankhula izi munzinda wa Lilongwe pamwambo okhazikitsa komiti imene akuyitcha kuti District Peace and Unity Committee imene cholinga chake ndi kulimbikitsa bata ndi mtendere munzindawu ndi madera akumidzi.
A Njirayafa anati komitiyi ithandizira kuchepetsa kusamvana kumene kumayamba kaamba ka kulimbirana malo komanso kusiyana pa zipembedzo ndi ndale.
Komishonala wa Malawi Peace and Unity Commission, a Francis Mkandawire, anati izi ndi zofunika kwambiri pa ntchito yoteteza ufulu wa nzika zimene zili ndi kuthekera kokhala ndi dziko la bata ndi mtendere.
“Dziko lathu ndi la mkaka ndi uchi komabe sipalephera kukhala kusamvana, ndi chifukwa chake tikuyenera kugwirana manja pa ntchito yolimbikitsa mtendere kuti tikhale ndi Malawi wokomera aliyense,” a Mkandawire anaonjezera.
Izi zikudza pamene dziko lino likuyembekezera kuchititsa zisankho zapatatu m’mwezi wa September chaka cha mawa.
Olemba: Thokozani Jumpha