Malawi Broadcasting Corporation
News Nkhani

John Okafor (Mr Ibu) wamwalira

Katswiri pankhani yochita zisudzo zapakanema mdziko la Nigeria, John Ikechukwu Okafor, yemwe amatchuka ndi dzina loti  Mr Ibu, wamwalira munzinda wa Lagos.

Malinga ndi nyumba zoulutsa mawu m’dzikolo, malipoti akuchipatala akusonyeza kuti nthenda ya mtima kapena kuti  Cardiac Arrest ndiyo yatengera katakweyu kulichete loweruka.

Malipotiwa akusonyezanso kuti Mr Ibu wakhala akuvutika ndi ndinthenda yakutseka kapena kuuma kwamagazi m’misempha kufikira pomwe chaka chatha akubanja analengeza kuti mwendo wakatswiriyu wadulidwa ngati mbali imodzi yopulumutsa moyo.

Malinga ndi mkulu wa bungwe loona za anthu ochita zisudzo m’dziko la Nigeria la  Actors Guild of Nigeria, a Emeka Rollas Ejezie, Mr Ibu asiya mkazi ndi ana atatu.

Mr Ibu amwalira ali ndi zaka 62 ndipo anaoneka mumafilimu  oposa 200 m’dziko la Nigeria.

Related posts

UK grants Malawi about K7BN to help those affected by El Nino

Rabson Kondowe

Mfumu yaikulu Mkukula yayamika boma kaamba ka chitukuko cha madzi ammipopi

Rabson Kondowe

Elephants threaten food security for Mchinji community

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.