Njonda ina iba mabelo afodya
Njonda ina ya m’mudzi mwa Bwananyambi m’boma la Mangochi yathawa anthu ataituluki kuti inaba mabelo a fodya kwa mu mlimi wina.
Apasula banja kamba kachimasomaso
Mayi wapa mudzi wina m’dera la mfumu Symon m’boma la Neno wapasula banja ndi manja ake kamba ka khalidwe lake lachimaso-maso.
Nkhandwe likolowola maso amkulu wina
Mwamuna wapa mudzi wina kwa Mazengera m’boma la Lilongwe ali mu ululu woopsya nkhandwe itamukolowola maso usiku ataledzera.
Anyamula maliro pa kaliyala
Mikoko yogona yapa mudzi wina ku Mtunthama mboma la Kasungu yaima mitu ndi zomwe wachita m’nyamata wina ponyamula malilo abambo ake pa kaliyala ya Njinga ya moto.Nkhani-yi ikuti m’nyamatayo ali ndi golosale ndipo masiku apitawa wakhala akuyenda ndi mkulu wina wa zitsamba pamene bambo ake amadwala mchipatala.