Amubwatika kuti amanga naye ukwati
Mai wina wa zaka 32 wapa mudzi wina m’boma la Phalombe akulira mosatonthozeka mnyamata wina wapa mudzi wa Magaleta kwa Mlauli m’boma la Neno atamubwatika kuti akumufuna ukwati ndikuti afike ku mudzi kwa mwamunayo.
Agwededza mudzi kamba ka chimasomaso
Mayi wina wapa mudzi wa Kamoto kwa Mabuka m’boma la Mulanje, wagwededza mudziwo ndi midzi ina yoyandikana kamba ka khalidwe lake lachimaso-maso.
Akunthana kamba ka ganyu yowaza nkhuni
Anyamata awiri omwe amagwira maganyu pamsika omwe uli kuseri kwa Chipatala cha gulupu mu mzinda wa Blantyre anakunthana mpaka kung’ambirana zovala kamba kolimbirana ganyu yowaza nkhuni.
Aphuluphuthidwa mpaka kukomoka
Mnyamata wina wa mtauniship ya Ndirande mu mzinda wa Blantyre amukuntha mpaka kukomoka atamupezerela akuba kompyuta mu ofesi ina ku Limbe mu mzinda wa Blantyre.