Akomoka ndi mowa kuntchito
Ntchito zinasokonekela pa kampani ina yopanga bisiketi mu mzinda wa Lilongwe mwamuna wina atakomoka ndi mowa.
Afuna kumangililidwa mumtengo akamwalira
Anthu ena mdera la Ndamera mboma la Nsanje akukhala mwa mantha ndi zomwe anachita Gogo wina wokhwima yemwe anauza anthu kuti akadzamwalira asadzalowe m’manda ati m’malo mwake adzangomumangilira mu mtengo.
Mkazi wamitala atentha udzu wa mkazi nzake
Mkazi wina yemwe ali pa mitala pa mudzi Chidula kwa Mangwazu m’boma la Kasungu amulamula kuti alipire mkazi m’nzake katundu komanso mitolo ya udzu 100 yomwe anayitentha.
Akuntha mkulu wawo ndi mpini
Anthu apa mudzi wina m’dera la Mfumu Cheku-cheku m’boma la Neno ndi wokhumudwa kwambiri ndi zomwe yachita nyakwawa yawo pokuntha ndi mpini mkulu wabwalo mpaka maganizi kuyendelera ngati madzi.