Nkahniyi ikuti m’mudzimo munali mwambo wa zochitikachitika zomwe anakonza a bungwe lina lazachitukuko. Pa mwambowo anakonza magule osiyanasiyana kuphatikizapo tchopa. Tsono mkaz wa mkuluyo atamva za mbowo anaganiza zopita komweko ncholinga choti akavine nawo guleyo. A Tchopa atalowa m’bwalo mayiyo anatengeka mtima mpaka analowa m’bwalomo ndipo mkulu wina yemwe amavina mwa kaso anamupanilira mayiyo posalabadira kuti ndi mkazi wa mwino. Mkuluyo ataona izi anangochoka pa bwalolo ndipo apa mpamene anathu anadziwiratu kuti yalakwa. Anthu ena anamukodola mayiyo kumuuza kuti mwamuna wake wanyanyala koma mayiyo akuti sanaimve mpaka guleyo anatuluka m’bwalo. Atakafika ku nyumba mayiyo anafikira m’naja kumuthobotsa ndi zibakera mpaka anathawa pa nyumbapo kukagona kwa achibale. Pakadali pano banjalo lakhululukirana koma akuti mwamunayo walamula kuti mayiyo asadzapezekenso akuvina pa mwambo uli wonse m’mudzimo.
Mbava ikunthidwa itagwidwa ikuba chimanga
Mbava ina yotchuka ya m’mudzi mwa Mandolo m’dera la Mfumu Kanduku mboma la Mwanza yaona zakuda atayikuntha kodetsa nkhawa pamene anayipeza ikuba chimanga m’munda mwa eni. Nkhaniyi ikuti m’mudzimo muli mkulu wina yemwe ambiri amamudziwa kuti ndi tsinzinantole. Kwa nthawi yaitali wakhala akuzunguza m’mudzimo komabe anthu amangodikira kuti lidzamukwanire la 40. Sabata yathayi mkuluyo anatasa kuba chimanga m’munda wina koma mwatsoka anthu ena odutsa m’njira anamuona. Anthuwo anamuzembelera nkumugwira ndipo apa sanayembekeze mwini mundawo koma kungoyamba kumuphika kwinaku akukuwa. M’mene anthu ena amatulukira kumundako anamupeza mkuluyo ali thapsya. Anthu ena achifundo ndi omwe anamukwekweza kupita naye kwawo ndipo mwini mundawo atamva anayamika kwambiri anthuwo. Kuyambira pa tsikulo Mbavayo ikungobuula mnyumba ndipo yalumbira kuti siidzabanso ati kamba koti yaona kuti anthu am’mudzimo ndi olimba mtima akhoza kudzamupha.