Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Illovo ithandiza okhudzidwa ndi kusefukira kwa madzi ku Nkhotakota

Anthu amene anakhudzidwa ndi ngozi ya kusefukira kwa madzi chaka chino ku Dwangwa m’boma la Nkhotakota alandira katundu osiyanasiyana wa ndalama zokwana K100 million kuchokera ku kampani ya Illovo sugar.

Loya wa kampani ya Illovo, yemwenso amayang’anira zofalitsankhani, a Maureen Kachingwe, anati anapeza thandizoli kuchokera ku South Africa ndi maiko ena a ku Ulaya.

M’modzi mwa akuluakulu ku kampaniyi, a Jeromy Ngolombe, apemphanso anthu okhudzidwa kuti alimbikitse ntchito zobzyala mitengo, zomwe ati zili ndi kuthekera kobwezeretsa chilengedwe m’dziko muno.

Wina mwa katundu yemwe apereka ndi zofunda, mapoto komanso zakudya.

Anthu asanu ndi omwe anamwalira pa ngoziyi ndipo anthu oposa 14,000 ndi amene anakhudzidwa ndi madzi osefukirawa m’mwezi wa February chaka chino.

Olemba: Thokozani Jumpha

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

BJ commends SRWB management for dedication

MBC Online

Anglican Women urged to protect girls’ health

Arthur Chokhotho

CHAKWERA INAUGURATES SCHOOL of LAW, ECONOMICS & GOVERNMENT

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.