Boma, molumikizana ndi bungwe la UNDP, lakhazikitsa ntchito ya gawo lachiwiri komanso lachitatu ya Green Economic Transformation Facility (GETF).
Ntchitoyi ikupereka danga kwa anthu komanso kampani zomwe zili ndi maganizo akuya a ntchito zamalonda zothandizira kuchepetsa mavuto odza kaamba kosintha kwanyengo.
Poyankhula pamwambo okhazikitsa magawo awiriwa munzinda wa Lilongwe, mlembi mu unduna oona zachilengedwe komanso kusintha kwanyengo, a Yusuf Nkungula, anati kudzera mu ntchitozo, amayi komanso achinyamata akhala ndi mwayi opeza ntchito mbali inayi akudzidalira pa chuma.
Mkulu wa bungwe la UNDP Malawi, a Fennela Frost, ati ntchito yothetsa mavuto akusintha kwanyengo ndi yofunika mgwirizano pakati pa mabungwe amene siaboma ndi boma kuti ntchitoyi ikhale yatanthauzo.
Kudzera mumagawo awiriwa, munthu akhoza kukhala ndi mwayi olandira $300,000 (zomwe ndi zopyola K500 million) zogwilira ntchitozo.
Izinso zili chomwechi ndi kampani zimene zilembe mfundo ndi njira zapamwamba zamabizinesi zokhudza kulimbana ndi kusintha kwanyengo.
Mayiko a Germany komanso Flanders ndi amene akuthandiza magawo awiri kudzera ku UNDP, yomwe ikuyendetsa ntchito za GETF.