Malawi Broadcasting Corporation
Development Environment Local Local News Nkhani

DoDMA ilimbikitsa chitukuko cha madzi aukhondo

Anthu opyola 8,000 m’ma boma a Mulanje ndi Phalombe tsopano ali ndi madzi aukhondo kutsatira chitukuko chimene nthambi ya DoDMA yachita m’madera a Kamwendo ndi Misewufolo m’maboma awiriwa.

Ntchito yogawa madzi a m’mipopiyi, amene akuwapopa ndi mphamvu yadzuwa,ayigwira pansi pa Post Cyclone Idai and Kenneth Emergency Recovery and Resilience Project.

Wapampando wa komiti yoyendetsa chitukukochi kwa Kamwendo, a Blessings Mikeas, anati izi zithandiza kwambiri chifukwa madzi am’mijigo mderali amatuluka amchere.

M’modzi wa akuluakulu a Dodma, a Moses Chimphepo, anati zitukuko zotere zachitika m’maboma asanu ndipo anthu a mmaderawa atenge umwini wa chitukukochi kuti chikhalitse.

Kwinanso kumene DoDMA yachita chitukukochi ndi maboma a Chikwawa, Zomba ndi Nsanje.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Internal auditors hand over toilets to Nsala CDSS

MBC Online

TANZANIA MAIZE IMPORT BAN LIFTED

MBC Online

MOC hosts Sports Administration Course

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.