Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

CHUMA CHA MALAWI CHIKWERA NDI 3.3 PERCENT CHAKA CHINO – IMF

Nduna ya zachuma a Simplex Chithyola Banda ati zomwe lanena bungwe la zachuma padziko lonse la IMF kuti chuma cha dziko lino chikwera ndi 3.3 percent chaka chino, zaonetseratu kuti ndondomeko zachuma tsopano zayamba kuyenda bwino m’dziko muno.

Chaka chatha, chuma cha dziko lino, chinakwera ndi 1.6 percent.

A Chithyola-Banda ati izi zaonetseratu kuti mfundo zomwe boma linaika pothana ndi mavuto a zachuma m’dziko muno, zikubereka zipatso zabwino.

A Chithyola-Banda

Iwo ati kukwera kwa chuma komwe bungwe la IMF lalengeza, kufikila munthu aliyense zomwe zithandize kuti aliyense awone kusintha pa moyo wake.

Akuluakulu a bungwe la IMF anali m’dziko muno kwa masiku atatu motsogozedwa ndi a Mika Saito pomwe amazakambilana ndi akuluakulu a boma.

Nthumwi za bungaeli zinaonanso momwe boma likuyendetsera dongosolo komanso mfundo zobwezeretsa chuma m’chimake kutsatira ndalama zomwe bungweli linapereka kudziko lino zothandiza kukonzanso chuma chake.

Wolemba: Arthur Chokotho ndi Blessings Kanache.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

NEEF yapereka feteleza wa ngongole kwa alimi

MBC Online

Scorchers lero imwemwetera

Paul Mlowoka

Tidziganizira momwe tingatukulire maanja athu — Kunkuyu

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.