Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani Sports

CHIKHO CHA CHAMPION KABVINA CHAFIKA PA K20 MILIYONI

Kukhala nkoke-nkoke pakati pa matimu mu mpikisano wa Champion Kabvina chaka chino pomwe ndalama zomwe matimu amalimbirana zakwera kuchoka pa K13 miliyoni kufika pa K20 miliyoni.

Ziphadzuwa kuonetsa Chikho pa masewero omaliza mu mpikisano oyamba.

Omwe amathandiza mpikisanowu a King Msaiwale Kabvina omwenso ndi mwini wake wa bwalo la za masewero la Champion ku Mponela ati mpikisanowu uyamba pa 7 April ndipo udzatha pa 27 October chaka chino.

A Kabvina ati mphotho zopita kumatimu zakwezedwanso pomwe opambana adzilandira K7.5 milluyoni kuchoka pa K3.5 miliyoni, wachiwiri K3.5 miliyoni kuchoka pa K2.5 miliyoni, wachitatu K2.5 miliyoni kuchoka pa K1.5 miliyoni pomwe timu yachinayi idzalandira K1.5 miliyoni kuchoka pa K750,000.

Timu ya Wanderers reserve idakhala akatswiri mu mpikisano oyamba

Chikho cha Champion chinayamba chaka chatha ndipo timu ya Mighty Mukuru Wanderers Reserve ndiyo inakhala akatswiri.

 

Wolemba: Emmanuel Chikonso.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Ophunzira ena a Form Four achedwa kulemba mayeso awo lero

MBC Online

NRB yalemba anthu opyola 12 million

Trust Ofesi

‘Mukapezeka ndi Chamba mumangidwa’

Rudovicko Nyirenda
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.