Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

Chigamulo ndi mawa — Hara

Sipikala wa Nyumba ya Malamulo, a Catherine Gotani Hara, wati apereka chigamulo mawa paza mpungwepungwe umene unali m’nyumbayi akachita zokambirana ndi akuluakulu ena.

Lachinayi, a Bester Awali, omwe ndi phungu otsutsa wadera la pakati m’boma la Zomba, anaponya botolo la madzi lomwe linagwera kumbali ya Boma, zomwe zinapangitsa a Hara kunena kuti khalidweli ndi loyipa.

Izi zimachitika pamene a Joshua Malango, phungu wa pakati cha kum’mvuma kwa boma la Dedza, anapempha a Sameer Suleiman kuti achotsedwe ngati wa pampando wa komiti yoona za malimidwe kaamba ka khalidwe loyipa.

Nkhaniyi inayamba cha kum’mawa ndipo inapitilira mpaka masana, zomwe zinachititsa kuti aphungu aweruke mochedwa.

#MBCDigital
#Manthu

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Wives of MDF soldiers urged to participate in sports

Rudovicko Nyirenda

Court grants stay order on release of Chinese involved in Wildlife Crimes and Money Laundering

Mayeso Chikhadzula

Malawi benefits from UK child development programme

Paul Mlowoka
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.