Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Bande apempha mafumu atsogolere chitukuko

Phungu wadera la Blantyre City East, a John Bande, wapempha mafumu kuti akhale patsogolo poteteza zipangizo ndi katundu wa boma pomwe akulimbikitsa ntchito zachitukuko.

A Bande anena izi pa mwambo olonga a Horace Chilembwe kukhala Group Village Headman Nanthoka ku Machinjiri ku Blantyre.

John Bande, Phungu wadera la Blantyre City East

Iwo anatchulapo malo a Machinjiri Chitukuko Centre pomwe boma likumangapo chipatala ndi sukulu ndi zina, kuti akufunika kuwateteza kuti anthu ena asalowelere.

Ena mwa athu omwe anali nawo pamwambowu ndi mlembi wamkulu ku unduna wa zachuma, a Betchani Tchereni,  kudzanso anthu omwe akufuna kudzapikisana nawo pachisankho ngati phungu omwe ndi a Deus Sandram “Bwande”, Alex Chimwala komanso a Chisawa Mbewe.

Related posts

RBM Introduces 50, 20 Kwacha coins

McDonald Chiwayula

USAID yatsanzika mwapamwamba ku Fisheries

Alinafe Mlamba

‘Yambani ma bizinesi ang’ono ndi mtukula pakhomo’

Yamikani Simtowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.