Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Awagwira komwe amabisala

Apolisi ku Soche mumzinda wa Blantyre amanga amuna ena awiri, kuphatikiza pa atatu omwe anawagwira kale mwezi wa March, pa mlandu wakuba ndikuvulaza munthu ku Soche East mumzinda womwewo.

Ofalitsankhani wapolisi ku Soche, Aaron Chilala, wati awiriwo, omwe awagwira ku Nsanje komwe amabisala, ndi John Washen wazaka 57 ndi James Basopa wazaka 37, ndipo awapezanso ndi zipolopolo 12.

A Chilala ati awiriwo, pamodzi ndi ena atatu omwe akuwasunga ku ndende ya Chichiri, anapita kunyumba ya Alex Makanjira ku Soche East, omwe anawaombera ndi mfuti yamtundu wa AK-47 kenako anaba katundu wa mnyumba ndi ndalama zokwana K100, 000.

Apolisi anakwanitsa kupeza katundu wina wobedwayo komanso anapeza mfuti yomwe anthuwo amagwiritsa ntchito.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MZUNI alumni yapereka K2.9M kwa ophunzira osowa

MBC Online

Ogonana okhaokha chigamulo mawa

MBC Online

Awamanga powaganizira kuti amafuna kulowetsa chamba ku ndende

Charles Pensulo
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.