Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Atsiriza kufufuza za imfa ya anthu asanu ku Blantyre

A polisi ati katswiri opima matupi aanthu, Charles Dzamalala, watsiriza kupima matupi a anthu omwe  afa atamwa mowa wina kwa Manase ku Blantyre.

Mneneri wa apolisi mchigawo chakummwera, Joseph Sauka, wati zotsatirazi azitulutsa nthawi ina iliyonse.

A Sauka ati anthu asanuwa anamwalira mmodzi mmodzi atamwa mowawu, zomwe zinachititsa achipatala kuyamba ayimitsa kuti awiri mwa matupi a anthuwo asawaike mmanda kuti awapime kaye.

Anthu omwe anamwa mowawu, malinga ndi a Sauka, analipo asanu ndi atatu ndipo awiri ali mwakayakaya pomwe mmodzi akuwonetsa kusintha.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Lake Malawi’s volume increases by 44 centimetres — NWRA

Romeo Umali

Parliament, Chamkakala to continue meeting this afternoon

Aisha Amidu

Principal Secretaries are key in implementing Govt’s policies — Zamba

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.