Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Apindula ndi ulimi wa mpunga ku Mzimba

A Mapulani Nkosi aku Mzimba akusimba lokoma kaamba kochita ulimi wa mpunga m’bomali, lomwe ambiri amalidziwa ndi ulimi wa fodya komanso mtedza.

Nkosi

A Nkosi, amene ali ndi zaka 34, ati akhala akulima mpunga kwa zaka zitatu tsopano.

“Ine chidwi changa chinabwera pomwe ndinapita ku Karonga kukacheza komwe ndinaona anthu akulima mpunga, ndipo ndinaganiza zophunzirako ziwiri zitatu kuti ndikayesere kwathu,” a Nkosi analongosola.

Nkosi wati atafika kwawo anapeza malo ndikudzala mpunga ndipo pano amakolora ma tini pafupifupi 30.

Pakadali pano, Nkosi wapempha akuluakulu owona za ulimi kumpoto kwa boma la Mzimba kuti ayambe kuthandiza alimi ampunga komanso ena onse omwe aonetsa chidwi ndi ulimiwu ndi upangiri wa momwe angasamalire mbewu zawo komanso kupeza phindu lochuluka.

 

M’mau ake, mmodzi mwa akuluakulu ku Mzuzu ADD, a Anderson Chikomola, wati ndizopatsa chidwi komanso kulimbikitsa kuona alimi m’bomali akulima mbewu zosiyanasiyana.

Olemba George Mkandawire

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Dr Chakwera apereka K5 million zothandizira pamaliro a Kasambara

Chisomo Manda

Gawo lachiwiri la filimu ya Sinister Bonds alitulutsa

Simeon Boyce

Mbali ina ya msewu wa Chiwembe sanamange bwino — Chimwendo Banda

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.