Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Aphana chifukwa cha chibwenzi

Apolisi ku Chiradzulu akufufuza Madalitso Chikondi, wazaka 18, pomuganizira kuti anapha mnzake Innocent Masamba,18 yemwe amamuganizira kuti amazembera chibwenzi chake.

Lovice Mulinde, yemwe ndi wachiwiri kwa ofalitsankhani wa Polisi ya Chiradzulu, wati malemu Masamba anali pasitolo ya Makiliyere komwe amakaonera maimbidwe ena ndipo Chikondi adayamba kumenya ndi kulasa mnzakeyu ndi mpeni ndipo anafera pompo.

Chikondi amachokera m’mudzi wa Mtambo kwa mfumu yayikulu Machinjiri mu mzinda wa Blantyre pomwe Masamba adali ochokera m’mudzi wa Ulaya, kwa mfumu yayikulu Mpama m’boma la Chiradzulu.

 

Related posts

Child education advocate calls for trained caretakers

Romeo Umali

NBS re-commits to supporting sports

MBC Online

President Chakwera calls on religious leaders to support environmental restoration efforts

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.