Anthu omwe anali mamembala a chipani cha DPP okwana 619 ochokera m’madera a kummwera komanso pakati m’boma la Mulanje, alengeza kuti atuluka chipanichi ndipo alowa Malawi Congress (MCP).
Mmodzi wa akuluakulu a MCP, a Brown Mpinganjira, Wapampando wa chipanichi ku Mulanje komanso wachiwiri kwa mkulu wa achinyamata mchipani cha MCP, a Blessings Chilembwe, ndiwo alandira anthuwa pamwambo umene unachitika pa Mulanje paboma.