Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Anthu a ku Ntcheu ndiwothokoza – Nyakwawa Gwedeza

Nyakwawa yayikulu Gwedeza yaku Ntcheu yati anthu m’bomali ndiwokondwa ndi chitukuko chokulitsa msewu wa M1 pa Kampepuza.

A Gwedeza ati mwachitsanzo, chifukwa cha kuonongeka kwa msewu, pa msika wa Kampepuza pamachitika ngozi zomwe tsopano zikuyembekezeka kuchepa.

Pa Kampepuza ndi amodzi mwa malo odziwika bwino m’boma la Ntcheu kaamba ka msika omwe umachitika lachisanu lililonse.

Ntchito yokonzanso ndikukulitsa msewuwu inayamba mu September chaka chatha ndipo ikuyembekezeka kutha mu November chaka chino.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Burning Spear atsanzikana ndi anthu asanapume kuimba

Emmanuel Chikonso

A Chakwera alibe tsankho — Chimwendo Banda

Mayeso Chikhadzula

Dziko la Malawi lili ndi mwai waukulu woonjezera Mphamvu zamagetsi

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.