Malawi Broadcasting Corporation
Development Environment Local Local News Nkhani

Alimbikitsa anthu kupha makwacha kuchokera ku zinyalala

Mmodzi mwa akuluakulu ku bungwe lowona zakasamalidwe kazinyalala la Waste Advisors, a John Chome, ati dziko la Malawi lili ndikuthekera kopeza phindu lochuluka kuchokera ku zinyalala.

A Chome anena izi mumzinda wa Lilongwe pamene amafotokozera atolankhani pazokonzera za msonkhano wawo waukulu wolimbikitsa anthu kasamalidwe kazinyalala, omwe udzachitike pa 27 March chaka chino ku Bingu International Convention Centre (BICC) mumzinda wa Lilongwe.

A Chome ati anthu akuyenera kusintha kaganizidwe kuti zinthu zakutha ntchito sizingagwirenso ntchito, ndipo anati kaganizidwe kotere kakuthandizira kuwononga chilengedwe.

“Zinyalala za pakhomo monga zakudya zotsala, makoko ambatata ndi zina zimapanga manyowa amphanvu omwe angathandize kubwezeretsa chonde mnthaka,” anatero a Chome.

Bungwe la Waste Advisors likugwira ntchito ndi a mabungwe, ochita malonda, makhonsolo mwa ena pofuna kudziwitsa anthu phindu lomwe lingapezeke kuchokera ku zinyalala.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

‘Tileke kugwiritsa ntchito mapepala opyapyala’

Lonjezo Msodoka

MBC for continued collaboration with DIOs

Timothy Kateta

Former bank teller nabbed for robbing ex-girlfriend at work

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.