Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Agwetsa sitolo zomangidwa malo osavomerezeka

A khonsolo yamzinda wa Lilongwe, mogwirizana ndi asilikali achitetezo, agumula ndikusalaza sitolo zimene zinaamangidwa mphepete mwa manda ku dera la Nsungwi ku Area 25 ku Lilongweko.

Malinga ndi anthu amene atitsina khutu, izi zachitika kum’bandakucha walero loweruka.

Asanagwetse pa maoneka chonchi. 
Atagwetsa pa maoneka chonchi.

M’mbuyomu, anthu okhala mderali adakachita zionetsero ku ofesi za khonsolo yamzindawu ndikuopseza kuti achitapo kanthu ngati akuluakulu akhonsoloyi sakagwetsa sitolozi.

Iwo ankadandaula kuti sitolozi zidamangidwa kufupi kwambiri ndi manda.

Kanema: Social media

#MBCOnlineServices

Related posts

Maranatha hails role of sports in academic excellence

McDonald Chiwayula

Legislator vows to enhance education standards

Romeo Umali

GOVT, MAMALAND, PRESS TRUST SIGN CARBON TRADING PACT

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.