Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

A Malawi adekhe pamene boma likumanganso misewu yolimba – Hara

A Jacob Hara, omwe ndi nduna ya za mtengamtenga, apempha anthu m’dziko muno kuti akhale odekha pamene boma likuyesetsa kukonzanso misewu.

Ndunayi yayakhula izi pomwe imayendera ntchito yomanga komaso kukonza msewu wa M1, kuchoka pa mphambano yopita ku Kamuzu International Airport ku Lilongwe kufika ku Kasungu mpaka kwa Jenda.

A Hara ati ndiokhutira ndi momwe ntchito yomanga msewuyi ikuyendera.

Mmodzi mwa akuluakulu ku Roads Authority, Engineer Joe Longwe, ati akulondoloza bwino lomwe nthawi yomwe anapatsana ndi ma kontrakitala omanga misewu ndi cholinga choti misewu ikhale yapamwamba.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Aloleni achinyamata kupereka maganizo ku DPP — Chimwendo Banda

MBC Online

‘Boma lithandiza onse’

MBC Online

Bungwe la Red Cross lapereka ndalama kwa mabanja okhudzidwa ndi kusefukira kwa madzi

Olive Phiri
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.