Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

A Dossi ayikidwa m’manda ndi mwambo wachisilikali

Mwambo oyika m’manda malemu Moses Dossi, omwe anaakhalapo olembankhani za masewero komanso nduna ya zamasewero mu ulamulo wa boma la chipani cha United Democratic Front, uli mkati m’mudzi mwa Kalimanjera kwa Chapananga m’boma la Chikwawa.

Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, walamula kuti malemu Dosi ayikidwe m’manda motsatira mwambo wa chisilikali popereka ulemu ku ntchito zawo.

Nduna yoona zamalo, a Deus Gumba, ndi amene akuyimilira prezidenti wa dziko lino.

A Dossi anamwalira lachinayi mmawa atadwala kwa nthawi yayitali.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Tilimbikitse chikhalidwe ndikusunga mbiri ya Malawi – MAGLA.

MBC Online

Bungwe la SFFRFM lati zokonzekera AIP zili m’chimake

Charles Pensulo

‘Ubale wa dziko la China ulimbikitse Malawi pa ntchito zamalonda’

Lonjezo Msodoka
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.