Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

A Chakwera ndagoma nawo — Mwambande

Phungu wadera la kumpoto m’boma la Karonga, a Mungasulwa Mwambande, wati chimene chachititsa kuti alowe chipani cha Malawi Congress (MCP) ndi zitukuko zimene President Dr Lazarus Chakwera akumwaza m’dziko muno mosayang’ana dera kapena zigawo.

A Mwambande, amene amayankhula ku Iponga pa msonkhano wandale powalandira m’chipanichi, ati anthu ochuluka mdera lawo ndi okondwa ndi utsogoleri umene ulipo pano, moti akufuna upitilire mpakana 2030 kuti dziko lino likhale losinthika.

Iwo anali a chipani cha Democratic Progressive ndipo anakhalapo wachiwiri kwa nduna yoona za migodi.

Mlembi wa chipani cha MCP, a Richard Chimwendo Banda, yemwe anali mlendo wolemekezeka pa mwambowu, anamema anthu kuti akhale pambuyo pa Dr Chakwera, omwe cholinga chawo ndi kusintha miyoyo ya anthu onse m’dziko muno.

Olemba: Musase Cheyo
Ojambula: Boston Tembo

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Bangwe All Stars garner over K16M in pledges

Nobert Jameson

Concern over illegal mining in Nkhotakota Game Reserve

MBC Online

CHAKWERA TO ATTEND SEVENTH DAY ADVENTIST BLANTYRE CENTENARY CELEBRATIONS

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.