Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

A Chakwera adzudzula m’chitidwe ozembetsa fodya

Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera wati ndi kofunika kuti chitetezo chikhale chokhwima pofuna kuthana ndi atambwali amene amazembetsa fodya kupita naye ku maiko akunja posafuna kulipira msonkho.

Dr Chakwera amayankhula izi m’boma la Kasungu potsegulira msika wa malonda a fodya ndipo anati lamulo ligwire ntchito pa mchitidwewu

“Tikupempha inu a Inspector General kuti gwirani tchito yothana ndi anthu amenewa,” anatero Dr Chakwera.

Mtsogoleriyu anayamikiranso ntchito yotamandika yomwe alimi a fodya akugwira pothandizira kuti dziko lino lidzipeza ndalama zakunja (forex).

Dr Chakwera alangiza anthu onse kuti azidzipereka pa ntchito zosiyanasiyana zothandiza kuti dziko lino lidzipeza ndalama zakunja ngati momwe akuchitira alimi a fodya.

Related posts

Nkhanza za m’banja zachuluka m’boma la Balaka – Apolisi

Rabson Kondowe

Tigwirane manja pothana ndi cancer ya m’mawere – Udedi

Rabson Kondowe

Masamba wabweza chipongwe kwa Tcheta

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.