Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

A Chakwera adzudzula m’chitidwe ozembetsa fodya

Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera wati ndi kofunika kuti chitetezo chikhale chokhwima pofuna kuthana ndi atambwali amene amazembetsa fodya kupita naye ku maiko akunja posafuna kulipira msonkho.

Dr Chakwera amayankhula izi m’boma la Kasungu potsegulira msika wa malonda a fodya ndipo anati lamulo ligwire ntchito pa mchitidwewu

“Tikupempha inu a Inspector General kuti gwirani tchito yothana ndi anthu amenewa,” anatero Dr Chakwera.

Mtsogoleriyu anayamikiranso ntchito yotamandika yomwe alimi a fodya akugwira pothandizira kuti dziko lino lidzipeza ndalama zakunja (forex).

Dr Chakwera alangiza anthu onse kuti azidzipereka pa ntchito zosiyanasiyana zothandiza kuti dziko lino lidzipeza ndalama zakunja ngati momwe akuchitira alimi a fodya.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

‘Akabaza kalembetseni m’kaundula wa voti’

Emmanuel Chikonso

Mlimi apata mphoto ya K10 million

Simeon Boyce

MANEPO yayamikira Madam Chakwera polimbana ndi nkhanza za anthu achikulire

Beatrice Mwape
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.