Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

A Chakwera adzudzula m’chitidwe ozembetsa fodya

Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera wati ndi kofunika kuti chitetezo chikhale chokhwima pofuna kuthana ndi atambwali amene amazembetsa fodya kupita naye ku maiko akunja posafuna kulipira msonkho.

Dr Chakwera amayankhula izi m’boma la Kasungu potsegulira msika wa malonda a fodya ndipo anati lamulo ligwire ntchito pa mchitidwewu

“Tikupempha inu a Inspector General kuti gwirani tchito yothana ndi anthu amenewa,” anatero Dr Chakwera.

Mtsogoleriyu anayamikiranso ntchito yotamandika yomwe alimi a fodya akugwira pothandizira kuti dziko lino lidzipeza ndalama zakunja (forex).

Dr Chakwera alangiza anthu onse kuti azidzipereka pa ntchito zosiyanasiyana zothandiza kuti dziko lino lidzipeza ndalama zakunja ngati momwe akuchitira alimi a fodya.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MPONDA NDI MPHUNZITSI WA SILVER STRIKERS

MBC Online

Tabitha Chawinga tsopano ndiwa Lyon

Foster Maulidi

Ligi ipitilira mwezi ukaooneka — Classic U-20 Volleyball

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.